31
Okondedwa CONTACT NAME dzina langa ndine NAME ndimagwira ntchito ku Cultural Survival, bungwe lomwe limagwira ntchito ndi anthu pofuna kuteteza malo, awo, ziyankhulo zawo, zikhalidwe zawo komanso ufulu wawo. Ndikukumemani kuti mukhale nafe poteteza ufulu wa anthu. Bungwe la Cultural Survival limakonza ma pologalamu aulere pa wayilesi padziko lonse pansi kuwadziwitsa anthu zoti ali ndi ufufu ochita zofuna zawo,ndikudziwitsidwa zinthu zinthu sizanachitike ngati magulu akunja akufuna kugwiritsa ntchito malo komanso zinthu zawo zisanagwiritsidwe ntchito. Tsatirani ndondomeko ya mapologalamu a pa wayilesi apa: LINK SPECIFIC SETS Uthenga wa mawu ulipo mu ziyankhulo zochepa koma tili ndi uthenga wolembedwa m’chichewa womwe waphatikizidwa. Ngati muli okondwa kuthandauzira mu chiyankhulo chomwe omvera anu angamve, tidzakodwa mutatitumiziranso mukathandauzira. Tikudikilira yankho lanu. Chonde yakhani ngati nyumba yanu yowulutsira mawu ili yokondwa kugwira nafe ncthito kapena ngati muli ndi mafunso aliwonse. Kuti mudziwe zambiri za bungwe la Cultural Survival, Chonde tipezeni pa: www.culturalsurvival.org Ndatha ine wanu NAME

culturalsurvival.files.wordpress.com  · Web view1. kodi. ufulu wochita ... ndi zithu za chilengedwe za m’dera mwathu, makamaka ngati ncthitozo zikhonza kubweletsa kusintha komanso

Embed Size (px)

Citation preview

Page 1: culturalsurvival.files.wordpress.com  · Web view1. kodi. ufulu wochita ... ndi zithu za chilengedwe za m’dera mwathu, makamaka ngati ncthitozo zikhonza kubweletsa kusintha komanso

Okondedwa CONTACT NAME

dzina langa ndine NAME ndimagwira ntchito ku Cultural Survival, bungwe lomwe limagwira ntchito ndi anthu pofuna kuteteza malo, awo, ziyankhulo zawo, zikhalidwe zawo komanso ufulu wawo. Ndikukumemani kuti mukhale nafe poteteza ufulu wa anthu.

Bungwe la Cultural Survival limakonza ma pologalamu aulere pa wayilesi padziko lonse pansi kuwadziwitsa anthu zoti ali ndi ufufu ochita zofuna zawo,ndikudziwitsidwa zinthu zinthu sizanachitike ngati magulu akunja akufuna kugwiritsa ntchito malo komanso zinthu zawo zisanagwiritsidwe ntchito.

Tsatirani ndondomeko ya mapologalamu a pa wayilesi apa: LINK SPECIFIC SETS

Uthenga wa mawu ulipo mu ziyankhulo zochepa koma tili ndi uthenga wolembedwa m’chichewa womwe waphatikizidwa. Ngati muli okondwa kuthandauzira mu chiyankhulo chomwe omvera anu angamve, tidzakodwa mutatitumiziranso mukathandauzira.

Tikudikilira yankho lanu. Chonde yakhani ngati nyumba yanu yowulutsira mawu ili yokondwa kugwira nafe ncthito kapena ngati muli ndi mafunso aliwonse.

Kuti mudziwe zambiri za bungwe la Cultural Survival, Chonde tipezeni pa:

www.culturalsurvival.org

Ndatha ine wanuNAME

Page 2: culturalsurvival.files.wordpress.com  · Web view1. kodi. ufulu wochita ... ndi zithu za chilengedwe za m’dera mwathu, makamaka ngati ncthitozo zikhonza kubweletsa kusintha komanso

1. kodi ufulu wochita zomwe mwafuna,komanso kudziwitsidwa zinthu zisanachitike nchani?

Oyankhula oyamba:

Kodi mukudziwa kuti ufulu,wochita zomwe mwafuna komanso kudziwitsidwa zinthu

zisanachitidwe nchani ?

Oyankhula wachiwiri:

Eya! Ndi ufulu oti boma likuyenera kutidziwitsa m’madera athu pa za migodi, zitsime za mafuta,

madzi ndi zitukuko zina ndi zina zomwe zingakhanzikitsidwe m’madera athu. Chinanso

n’chakuti boma likuyenera kutimvera ndi kulemekeza maganizo athu ndikugwirizana chimodzi

ncthitozo zisanayambidwe m’madera athuwa.

Okamba nkhani:

Kuti mudziwe zambiri pitani pa , cultural survival dot org slash consent[culturalsurvival.org/consent or cs.org/consent]

Page 3: culturalsurvival.files.wordpress.com  · Web view1. kodi. ufulu wochita ... ndi zithu za chilengedwe za m’dera mwathu, makamaka ngati ncthitozo zikhonza kubweletsa kusintha komanso

2. ufulu wa anthu a m’dera

Oyakhula oyamba:

Kuchokera pobadwa, munthu aliyense ali ndi ma ufulu ena omwe sangachotseledwe ndipo ngati

anthu a m’madera, tili ndi ufulu okhala, wachibadwidwe komanso wodziwitsidwa.

Oyankhula wachiwiri:

Sizimatengera kuti kaya ndiwe wadziko lanji, ufuluwu ndi wa tonse ndipo ukuyenera

kutsatilidwa pamene boma likufuna kuchita chilichonse ndi zithu za chilengedwe za m’dera

mwathu, makamaka ngati ncthitozo zikhonza kubweletsa kusintha komanso mavuto ku nthaka

yathu

Page 4: culturalsurvival.files.wordpress.com  · Web view1. kodi. ufulu wochita ... ndi zithu za chilengedwe za m’dera mwathu, makamaka ngati ncthitozo zikhonza kubweletsa kusintha komanso

3. kuwayimba milandu ma kampani

Oyankhula oyamba:

M’nyengo zonse ndimadandaula pa za kuchepa kwa zokolora zathu; tilibe minda yokwanira

kuyambira pomwe makampani adabwera ku dera kwathu.

Oyankhula wachiwiri:

Ndizoona, anatenga malo athu popanda chilolezo. Ufulu wachibadwidwe umatiteteze ife anthu

okhala m’madera ndipo limanenetsa kuti palibe ntchito yomwe ikuyenera kuchitika m’dera

mwathu popanda boma kapena ma kampani kutidziwitsa kaye, kutifunsa ndiponso kutimvera.

Tiyeni tichitepo kanthu kuwayimba mlandu makampani amenewa.

Okamba nkhani:

Page 5: culturalsurvival.files.wordpress.com  · Web view1. kodi. ufulu wochita ... ndi zithu za chilengedwe za m’dera mwathu, makamaka ngati ncthitozo zikhonza kubweletsa kusintha komanso

4. Atsogoleri

Oyankhula oyamba:

Ndine munthu wamba. Ndili ndi ufulu wochita zomwe ndafuna, ndi wodziwitsidwa zinthu

zisanachitike, koma boma limagwiritsa ntchito njira zambiri kuti liphwanye ufuluwu. Imodzi

mwanjirazi ndikupanga ziphuphu ndi mafumu, kuwapatsa ntchito, ndi malonjezo ena ndi ena

kuti achite zofuna za boma kapena makampani kusiya zofuna za anthu awo onse. Pa chifukwa

ichi, ndikwabwino kuti anthu adzisankha atsogoleri omwe amayikira kumtima mavuto a anthu

awo ndipo tidzigwira ntchito limodzi ndi atsogoleriwa potukula madera athu

Page 6: culturalsurvival.files.wordpress.com  · Web view1. kodi. ufulu wochita ... ndi zithu za chilengedwe za m’dera mwathu, makamaka ngati ncthitozo zikhonza kubweletsa kusintha komanso

5. Pangano la bungwe la UN, Gawo khumi

Oyankhula oyamba:

Kwa madera a anthu wamba, ufulu wachibadwidwe, kuchita chomwe wafuna komanso

kudziwitsidwa limalimbikitsidwa ndi gawo khumi la pangano la UN pa za ufulu wa anthu

wamba, lomwe limakamba kuti mayiko ndi maboma sangathamangitse anthu m’madera awo

kapena m’malo awo, ngakhale kuchita zomwe akufuna popanda chilolezo cha anthuwo.

Page 7: culturalsurvival.files.wordpress.com  · Web view1. kodi. ufulu wochita ... ndi zithu za chilengedwe za m’dera mwathu, makamaka ngati ncthitozo zikhonza kubweletsa kusintha komanso

6. Pangano la bungwe la UN, Gawo 19

Oyankhula oyamba:

(mawu a pansipansi) Gawo 19 la pangano la bungwe la UN pa za ufulu wa anthu a m’madera

limanena kuti (mawu omveka bwino bwino) boma likuyenera kulandira chilolezo kuchokera kwa

anthu lisanapange zilizonse zomwe zikhonza kuwasokoneza athuwo.

Page 8: culturalsurvival.files.wordpress.com  · Web view1. kodi. ufulu wochita ... ndi zithu za chilengedwe za m’dera mwathu, makamaka ngati ncthitozo zikhonza kubweletsa kusintha komanso

7. Madera a chitetezo

Oyankhula oyamba:

Monga anthu wamba, tili ndi ufulu okhala m’madera otetezedwa ndipo ngati kusitha

kungachitike m’madera mwathu, tiyang’ane gawo 29 la pangano la UN pa za ufulu wa anthu.

Panganoli limanena kuti: anthu am’madera akuyenera kupemphedwa komanso kuwuzidwa

zinthu zoopsa zisana sungidwe kapena kuponyedwa m’dera mwawo.

Page 9: culturalsurvival.files.wordpress.com  · Web view1. kodi. ufulu wochita ... ndi zithu za chilengedwe za m’dera mwathu, makamaka ngati ncthitozo zikhonza kubweletsa kusintha komanso

8. Ntchito za chitukuko.

Oyankhula oyamba:

(kuyankhulira pa chimkuza mawu) palibe kusintha komwe kungabweletsedwe

m’malo athu popanda kugwiritsa ncthito gawo 23 la pangano la UN pa za ufulu wa anthu lomwe

limanenetsa kuti boma likuyenera kupeza chilolezo kuchokera kwa anthu lisanavomereze ntchito

ina iliyonse ya chitukuko yomwe itha kuwasokonezera anthu nthaka yawo monga ntchito za

migodi, madzi ndi zinthu zina zotero.

Page 10: culturalsurvival.files.wordpress.com  · Web view1. kodi. ufulu wochita ... ndi zithu za chilengedwe za m’dera mwathu, makamaka ngati ncthitozo zikhonza kubweletsa kusintha komanso

9. Chithandizo Chochokera kunja

Oyankhula:

Monga anthu, tili ndi ufulu wosankha kusintha komwe kuti kuchitike m’dera mwathu. Monga

m’mene zinalembedwela mu pangano la bungwe la United Nations komanso gawo 169 la

bungwe lowona za anthu ogwira ntchito padziko lonse ndi ndondomeko zina zomwe

zimalemekeza ufulu wosakha zofuna komanso kudziwitsidwa. Ndondomekozi, zimalimbikitsa

ufulu wa anthuwu ndi kupempha mayiko kuti adzilemekeza ufulu wa anthu.

10. Ufulu wosatsutsika

Page 11: culturalsurvival.files.wordpress.com  · Web view1. kodi. ufulu wochita ... ndi zithu za chilengedwe za m’dera mwathu, makamaka ngati ncthitozo zikhonza kubweletsa kusintha komanso

Oyankhula oyamba:

Kwa anthu tonse, ufulu wochita zomwe tafuna, kudziwitsidwa zinthu zisanachitike ndi

wofunikira kwambiri, wachibadwidwe komanso osatsutsika. Izi zikuthandauza kuti, ndi ufulu

wofunika kwambiri ndi woyenera pa chitukuko ndipo sitingakane. Kutengera pa lamulo la dziko

lpnse lapansi, ufulu wochita zofuna ndi kudziwitsidwa zinthu zisana chitike ufuluwu

umawonetsetsa kuti anthu akuchita chisankho cha zitukuko zomwe akufuna mwaufulu kotero

kuti zipindulire iwo komanso mibadwo yomwe ikubwera kutsogolo molingana ndi chikhalidwe

chathu m’mene dziko lonse limaonera.

11. Kuphwanya ufulu wa anthu.

Page 12: culturalsurvival.files.wordpress.com  · Web view1. kodi. ufulu wochita ... ndi zithu za chilengedwe za m’dera mwathu, makamaka ngati ncthitozo zikhonza kubweletsa kusintha komanso

Control: Tinyimbo tomveka pansi pansi

Oyankhula oyamba:

Mwadzuka bwanji?

Oyankhula wachiwiri:

zikuyenda?

Oyankhula oyamba:

Chabwino zikomo. Mwamva zoti muli kampani yatsopano ntawuni? Ayamba

kulemba ntchito kwa anthu kuti ayambe zomanga manga m’mudzi mwathu muno.

Oyankhula wachiwiri:

chani? Sindimadziwa kalikonse…sindikukhulupilira zoti boma likupitilizabe

kupondereza ufulu wochita chomwe tafuna ndikudziwitsidwa womwe anthu ife tili nawo.

Akuyenera kutidziwitsa ndikumva maganizo athu ngati tikufuna chitukuko chimenechi

kapena ayi. Makamaka popeza kuti lamuloli ndilolembedwa momveka bwino

m’malamulo a dziko lino komanso malamulo a mayiko onse.

Oyankhula oyamba:

Inu ndiye mwanenetsa. Ndizachidziwikire kuti boma silikuchitapo kanthu

polimbikitsa izi. Ngati sitichitapo kanthu kuti boma lidzilemekeza ufulu wathu, maufulu

ndi malamulo omwe analembedwa adzingokhala penapake nkumachita fumbi

osamagwira ntchito yake. Makampani adzapitiliza kuphwanya ufulu wathu

ndikutengerapo mwayi kwa anthu wamba.

Oyankhula wachitatu:

Sitingalole ndipo sitidzalola kuti izi zichitike. Aphwanya ufulu wathu mokwanira.

Tiyeni timenyelele ufulu wathu poteteza dziko lapansi!

Page 13: culturalsurvival.files.wordpress.com  · Web view1. kodi. ufulu wochita ... ndi zithu za chilengedwe za m’dera mwathu, makamaka ngati ncthitozo zikhonza kubweletsa kusintha komanso

12. Thandauzo la kuchita chomwe ufuna

Control: Tinyimbo tomvekera pansi pansi

Page 14: culturalsurvival.files.wordpress.com  · Web view1. kodi. ufulu wochita ... ndi zithu za chilengedwe za m’dera mwathu, makamaka ngati ncthitozo zikhonza kubweletsa kusintha komanso

Oyankhula oyamba:

Ufulu wochita zomwe ufuna komanso kudziwitsidwa ndi ufulu omwe umakhudza

anthu onse pa nkhani za chitukuko m’madera athu.

Control: kanyimbo kopumira pang’ono (masekondi atatu)

Oyankhula wachiwiri:

Kuchita zomwe ufuna komanso kudziwitsidwa? Zikuthandauza chani mukamati

kuchita zomwe ufuna?

Control: kanyimbo kopumira pang’ono (masekondi atatu)

Oyankhula oyamba:

Gawo lochita chomwe ufuna limathandauza kuti boma silikuloredwa

kulowelerapo pa chisankho cha atsogoleri komanso anthu a m’madera chokhudza zoti

ngati akufuna zomanga manga m’dera lawo kapena ayi. Paazokambiranazi, anthu a

m’dera sangawumilizidwe mu njira iliyonse kuti avomereze maganizo ena ake. Izi

zikuphatikizapo kuwaopseza m’njira iliyonse, ziwawa, kugwiritsa ntchito udyo

mphamvu, katangale, ndi zina zotere. Ndizongofunika kuonetsetsa kuti pa zokambirana

zokhudza chitukuko pasakhale kuphwanya ufulu komwe tatchulaku kotero kuti boma

lidzilemekeza kwa ndthu ufulu wochita chome ufufna komanso kudziwitsidwa chinthu

chisana chitike..

Oyankhula wachiwiri:

Tikuyenera kuwumiliza kuti ufulu wochita chomwe tafuna ukhaledi woti

tidzichita chomwe tafuna.

13. Thandauzo la “Kudziwitsidwa zisanachitike”

Control : << phokoso la anthu pa zionetsero>

Page 15: culturalsurvival.files.wordpress.com  · Web view1. kodi. ufulu wochita ... ndi zithu za chilengedwe za m’dera mwathu, makamaka ngati ncthitozo zikhonza kubweletsa kusintha komanso

Oyankhula oyamba:

Galamukani! yimilirani! Palibenso nthawi ina yabwino kuposa ino kuti

tiwumilize boma kuti likhanzikitse ufulu wochita zomwe tafuna womwe unapelekedwa

kwa ife!

Control: kanyimbo kopumira pang’ono (masekondi atatu)

Oyankhula wachiwiri:

Mukudziwa, izi ndiye zikumveka. Zikhala kupita patsogolo kwakukulu ngati

boma lathu litavomereza za ufuflu wochita zomwe ufuna ndi kudziwitsidwa kwa

mtunthu. Chomwe chakhala chikusowa kwambiri ndi maganizo wodziwitsidwa chinthu

chisanachitike. Kudziwitsana kutachitika ntchito ya chitukuko isanayambe kapena

isanvomerezedwe ndi boma ndi njira. Zikuthandauza kuti tidzikhala ndi nthawi

yokwanira kwa anthu onse a m’dera kuti awunikire pa maganizo omwe apelekedwa.

Zoonadi! Tikuyenera kukhala ndi uthenga wokwanira ndinso womveka bwino

zitukukozi zisanayambe, kotero kuti titha kuzukuta ndikupanga maganizo athu ngati

anthu. Chinanso nchiyani, akuyenera adzigwira nafe ntchito limodzi pa gawo lililonse la

ntchitozo, mwachitsanzo pa kawuniwuni, kutsegulira komanso kutseka kwa ntchito za

migodi.

14. Thandauzo la "kudziwitsidwa”

Control: tinyimbo tomveka pansi pansi

Page 16: culturalsurvival.files.wordpress.com  · Web view1. kodi. ufulu wochita ... ndi zithu za chilengedwe za m’dera mwathu, makamaka ngati ncthitozo zikhonza kubweletsa kusintha komanso

Oyankhula oyamba:

Inu ndi ine, monga anthu okhala m’madera tili ndi ufulu wodziwitsidwa.

Control: kanyimbo kopumira pang’ono (masekondi atatu).

Ufuluwu ndiwofunikira pa chitukuko cha dera lililonse. Ichi ndi chifukwa chake

ukuyenera kukhanzikitsidwa kwa thunthu. Tiyeni tione zomwe zimathandauza tikamati

kudziwitsidwa. ‘Kudziwitsidwa’. Kukuthandauza kuti tili ndi ufulu olandira uthenga

wokwanira wokhudza chitukuko chomwe chikuyembekezeka kuchitika mu dera mwathu.

Izi zikuphatikizanso uthenga wokhudza ubwino ndi kuyipa ka ntchitozo ku za

chilengedwe komanso kwa anthu ndinso madera athu. Kafukufuku amene amachitidwa

pofuna kupeza uthengawu amatchedwa kuti “Environmental and Social Impact

Assessments”, kapena “ESIA” yemwe amayenera kuchitidwa ndi magulu oyima

pawokha wopanda m’gwirizano uliwonse ndi makampani. Uthenga wonse operekedwa

ukuyenera kukhala wokwanira, womveka bwino mchiyankhulo chathu, mogwirizana ndi

miyambo ndi chikhalidwe chathu ndi maganizidwe athu. Ndi udindo wathu kowonetsetsa

kuti ndife odziwitsidwa mokwanira maganizo omwe atha kukhudza anthu athu ndi malo

anthu asnapangidwe.

15. Ndiliti lomwe ufuluwu umagwira ntchito?

Oyankhula oyamba:

Page 17: culturalsurvival.files.wordpress.com  · Web view1. kodi. ufulu wochita ... ndi zithu za chilengedwe za m’dera mwathu, makamaka ngati ncthitozo zikhonza kubweletsa kusintha komanso

Mam’mawa wabwino, mulibwanji?

Oyankhula wachiwiri:

Ndili bwino zikomo. Eeh!, uli bwanji nkumano dzulo? Munakambirana zotani?

Oyakhula woyamba:

Zinalibwino kwambiri. Tinakambirana za ufulu wachibadwdwe, wochita zomwe

munthu ukufuna komanso wodziwitsidwa zinthu zisana chitike.

Oyankhula wachiwiri:

Koma chimenecho ndi chani? Mungafotokozeko zambiri?

Oyankhula oyamba:

Zimathandauza ufulu womwe anthu ife tili nawo kuti titetezere malo komanso

madera athu, ufulu womwe ndiwolembedwa m’malamulo woyendetsera dziko lino ndi

mayiko onse..

Oyankhula wachiwiri:

Ooh! chabwino, koma nanga tingawugwiritse ntchito bwanji ufuluwu? Ndipo

munyengo zotani?

Oyankhula woyamba:

Tikhonza ndipo tikuyenera kugwiritsa ntchito pa nthawi imene m’madera mwathu

mukuyembekezeka kuchitika zitukuko zosiyana siyana makamaka ngati pali chiopsezo

choononga chilengedwe. Popeza ndi ife amene timakhala m’maderawa komanso kuti

zotsatira zake zidzakhuza ife tomwe, zili ndi ife kuvomereza kuti zitukukozi zichitike

kapena ayi. Ufulu wachibadwidwe, wochita zomwe tafuna ndikudziwitsidwa kaye zinthu

zisanachitike umanenetsa kuti makampani akuyenera kutidziwitsa ndi kulemekeza

Page 18: culturalsurvival.files.wordpress.com  · Web view1. kodi. ufulu wochita ... ndi zithu za chilengedwe za m’dera mwathu, makamaka ngati ncthitozo zikhonza kubweletsa kusintha komanso

maganizo athu asanayambe kuchita chilichonse. Tikuyenera tiphunzire zambiri za izi.

Zikuwoneka ngati ndi zabwino kwambiri ku madera athu!

16. Udindo

Page 19: culturalsurvival.files.wordpress.com  · Web view1. kodi. ufulu wochita ... ndi zithu za chilengedwe za m’dera mwathu, makamaka ngati ncthitozo zikhonza kubweletsa kusintha komanso

Control: phokoso la kuchuna chuna kwa wayilesi (masekondi atatu)

Woyankhula woyamba:

Ufulu wachibadwidwe, wochita zofuna zathu komanso kudziwitsidwa chinthu

chisanachitike ndi ufulu womwe ife tilinawo monga anthu wamba pamene tikumenya

nkhondo yoteteza malo athu. Tikuyenera kukakamiza kuti ufulu wathu ulemekezedwe..

Control: kanyimbo kopumira pang’ono (masekondi atatu).

Oyankhula wachiwiri:

Agogo, tamverani zomwe akukamba pa wayilesi; kodi mukuganiza kuti ndi

chanzeru kwa anthu athu kuti amenyere nkhondo ufulu wathu wodziwitsidwa chinthu

chisana chitike?

Oyankhula wachitatu:

Ndi zoona, mwana wanga! Ufuluwu umateteza zinthu zathu zomwe; ufuluwu ubweletsa zabwino zambiri kwa anthu athu komanso dziko lonse lapansi. Dikira ndifotokoze: pogwiritsa ntchito ufulu umenewu, tikhonza kuteteza chilengedwe chathu ndikukhala ndi madzi a ukhondo ndo m’pweya wabwino zomwe zitha kuthandiza kuti mwina anthu athu adzikhala m’madera a ukhondo. Titha kuonetsetsa kuti ntchito za chitukukozi zitichitire ubwino osati kutiwononga.

Oyankhula wachiwiri:

Tsopano ndamvetsa Agogo! Izi ndi ndizothandiza kwabasi. Zikomo ko m’badwo wanu,

ndili ndi malo okhala aukhondo. Ndidzakwaniritsa udindo wanga wosamalira

chilengedwe kuti ndidzawasiyile ana anga komanso dzidzukulu malo abwino okhala.

17. Kugawanitsa ndi Kugonjetsa

Page 20: culturalsurvival.files.wordpress.com  · Web view1. kodi. ufulu wochita ... ndi zithu za chilengedwe za m’dera mwathu, makamaka ngati ncthitozo zikhonza kubweletsa kusintha komanso

Oyankhula woyamba:

Kugawanitsa ndi kugonjetsa. Ichi chakhala chida chomwe amakampani komanso

boma lakhala likugwiritsa ntchito pofuna kuchita zinthu m’madera. Ndi chimodzi mwa

dzitsanzo zomwe akhala akulephelera kulemekeza ufulu wa anthu wachibabwidwe

kuchita zofuna zawo komanso kudziwitsidwa chinthu chisana chitike. Malamulo a

padziko lonse akunenetsa kuti ma boma sakuyenera kutikakamiza kusintha maganizo,

miyambo ndi zikhalidwe zathu komanso njira zopangira ziganizo. Nthawi zambiri

makampani akulu akuluamayesetsa kupeza njira zophwanyila ufuluwu popeza amadziwa

kuti sitingavomereza zinthu zowononga chilengedwe ndi zomwe zitha kutisiya

m’mavuto. M’malo mwake amachita chinyengo ndi atsogoleri osiyana siyana m’madera

monga aphunzitsi, atsogoleri a mipingo, atsogoleri a ndale pogwiritsa ntchito uthenga

wabodza. Zittingasekelere zotere. Zili kwa ife kuonetsetsa kuti ufulu wathu

ukulemekezedwa kwathunthu. Sitidzalora kuti mtendere, umodzi komanso mphamvu za

mudzi wathu kuti zikhale pa chiopsezo chifukwa cha kugawikana ndi katangale.I

18. Mikumano ya m’madera

Page 21: culturalsurvival.files.wordpress.com  · Web view1. kodi. ufulu wochita ... ndi zithu za chilengedwe za m’dera mwathu, makamaka ngati ncthitozo zikhonza kubweletsa kusintha komanso

Oyankhula oyamba:

(mwachisoni) eeyi, zinthu zilibwanji?…

Oyankhula wachiwiri:

Zilibwino zikomo! Koma mukuwoneka wokhumudwa, chikuchitika ndi chiyani?

Oyankhula oyamba:

Ndakhumudwa kwambiri, ndakhala ndikumva mphekesera zokhudzana ndi

ntchito za migodi zomwe zakuyembekezeka kuchitika m’mudzi mwathu muno. Sibwino

popeza kuti anthu omwe akutsogolera sanatiuze ndikomwe zomwe zikuchitika.

Sakutsatira ufulu womwe tilinawo wochita zomwe tikufuna, komanso kudziwitsidwa

zinthu zisana chitike. Ndamvetsedwanso kuti boma likuyenera kukwaniritsa kwathunthu

ma ufulu amenewa ntchito za chitukuko ngati izi zikamachitika.x

Oyankhula wachiwiri:

Inu mukunena zoona. Tiyenera kuwonetsetsa kuti ufulu wathu ukulemekezedwa

potidziwitsa kaye ndikumva mbali yathu ntchito ngati izi zisanayambe. Mwachitsanzo pamene

ntchito ngati zomwezi zinabwera ku dera lakwathu, tinakumana ndikukambirana kuti tionetsetse

chilichonse chikamachitika ndipo tikuyenera kukhala ndi mphamvu zokwenyera makampani pa

zinthu zomwe adalonjeza ndi kuonetsetsa kuti akuchitadi ntchito zomwe tinagwirizana pa

zokambirana zathu. Ikanakhala ndondomeko yabwino kugwiritsa nchito m’dera lanu-

sitingapitilire kulolera kuti ntchitozi zipitilire ife tisakudziwapo kanthu

19. Zomwe ufulu wochita zofuna zathu, komanso kudziwitsidwa zinthu zisanachitike

umathandauza.

Page 22: culturalsurvival.files.wordpress.com  · Web view1. kodi. ufulu wochita ... ndi zithu za chilengedwe za m’dera mwathu, makamaka ngati ncthitozo zikhonza kubweletsa kusintha komanso

Oyankhula oyamba:

Kodi mukudziwa kuti ufulu wochita zofuna zanu, komanso kudziwitsidwa chinthu chisana

chitike umati chani?

Oyankhula wachiwiri:

Eya! Ndi ufulu womwe anthu wamba tilinawo wosankha chomwe tifuna kuti

chichitike pa malo athu.

Oyankhula oyamba:

Ndipo mukudziwa kuti titha kugwiritsa ntchito ufuluwu bwino lomwe m’madera

mwathu?

Oyankhula wachiwiri:

Hmm chabwino, koma sikweni kweni,

Oyankhula oyamba:

Monga anthu wamba okhala m’madera, ndi udindo wathu kufufuza uthenga

wokwanira wa ufulu umenewu, kotero kuti tisaponderezedwe ndi boma kapena

makampani. Kuti tipange ufuluwu kukhala woona, tikuyenera kumvetsetsa kuti ufuluwu

ndi wa anthu onse zomwe zikusonyeza kuti boma liyenera kulemekeza njira zomwe

timagwiritsa ntchito podziwitsana ndi kupanga zisankho za zomwe tikufuna.

Zikusonyezanso kuti oyimilira boma, makampani komanso midzi yathu akuyenera

kukumana pamodzi ndi kukambirana zokhudza chitukuko ndipo ife ndi amene tili ndi

mawu omaliza ndi cholinga chovomereza zitukuko zomwe zingapindulire madera athu.

20. Malangizo

Control: Nyimbo zamakolo pansi pansi

Page 23: culturalsurvival.files.wordpress.com  · Web view1. kodi. ufulu wochita ... ndi zithu za chilengedwe za m’dera mwathu, makamaka ngati ncthitozo zikhonza kubweletsa kusintha komanso

Oyankhula woyamba:

Kodi mukudziwa ndondomeko yomwe mukuyenera kutsatira kuti muonetsetse

kuti pali ufulu wochita chomwe mwafuna , komanso kudziwitsidwa chinthu

chisanachitike?

Control: kanyimbo kopumira pang’ono (masekondi atatu).

Oyankhula wachiwiri:

Kuti mudziwe kuti ufuluwu ndi wabwino kwa anthu tonse, tikuyenera kutsatira

ndondomeko izi pamene tikukumana ndi ntchito za chitukuko pa malo athu. Anthu

okhala m’maderawa akuyenera kudziwitsidwa kuyambira pa chiyambi. Nthawi

yokwanira ikuyenera kuperekedwa kuti dera lonse lilandire uthenga uliwonse wofunikira

wokhudza ubwino ndi kuipa kwa ntchito za chitukukozo ndi kupereka mpata kuti pakhale

zokambirana zikhudza mfundo zimenezi. Uthenga ukuyenera kuperekedwa pogwiritsa

ntchito njira zofalitsira uthenga zamakolo. Chiganizo chidzipangidwa popanda

kupondereza komanso kuopseza kwa oyang’anira chitukukocho. Zonse zomwe

mwagwirizana zikuyenera kulembedwa nd ikusungidwa bwino. Ngati ufulu

utaphwanyidwa kumbukuirani kuti pali njira zomwe tithakugwiritsa tchito pofuna kupeza

thandizo pa za kuphwanyidwa kwa ufuluwu pa dziko lonse lapansi kuchokera ku

mabungwe monga la United Nations.

Kuti mudziwe zambiri pitani pa. cultural survival dot org slash consent

[culturalsurvival.org/consent or cs.org/consent]